15/05/2025
KODI MWADZUDZULIDWA KANGATI...?
📖 MIYAMBO 29:1 "Yemwe aumitsa nkhosi atadzudzulidwa kwambiri, adzasweka modzidzimuka, palibe chomchiritsa"
Choyamba ndimafuna ndi kuuzeni kuti mau oti "KUDZUDZULIDWA" amatathauzo "Kumuuza Mzako Kuti Asiye Mankhalidwe Oyipa Omwe Angamubweretsere Mavuto Mzakoyo,"
Muyenera kuzindikila kuti CHIKONDI ndi chimene chimamupangitsa munthu kuti "afike pomudzudzula mzake yemwe akuchita makhalidwe oipa omwe angamubweretsere mzake ochita zoipayo mavuto"
📖 Chibvumbulutso 3:19 "Onse amene ndiwakonda, NDIWADZUDZULA ndi kuwalanga; potero chita changu, nutembenuke mtima"
Pa 📖 Chibvumbulutso 3:19 tikupeza kuti, MULUNGU anthu amene amawakonda AMAWADZUDZULA kuti asiye uchimo, ndipo chomwe chikumupangitsa MULUNGU kuti afike pomudzudzula munthu ndi chifukwa chakuti MULUNGU amakhala wawoona zowawa ndi zowoopsa zomwe munthuyo adzakumane nazo akadzaponyedwa ku Gahena.
Ndithu MULUNGU chifukwa chomukondetsetsa munthu, nthawi zonse IYE akamuona munthu akuchimwa MULUNGU amachita changu kumudzudzula muthu wochimwayo pofuna kuti asiye uchimowo ndicholinga chakuti munthu ochimwayo asakapezeke ku Gahena.
📖 Miyambo 29:1 "Yemwe aumitsa nkhosi atadzudzulidwa kwambiri, adzasweka modzidzimuka, palibe chomupulumutsa"
Baibulo pa 📖 Miyambo 29:1 likuwulura chisisi chakuti "MUNTHU OCHIMWA AMENE ADZUDZULIDWA MAULENDO OCHULUKA KOMA OSAFUNA KULAPA, ZOTSATILA ZAKE ZIMAKHALA MUNTHU OCHIMWAYU KUPONYEDWA KU GAHENA"
Mfuso Mkumati "Kodi ndi chifukwa chiyani anthu omwe alandira chidzudzulo maulendo ochuluka zedi, zotsatila zake zimakhala anthu otere kuponyedwa ku Gahena...?
YANKHO LIKUPEZEKA PA 📖 AROMA 1:28
📖 Aroma 1:28 Ndipo monga iwo anakana kukhala naye MULUNGU m'chidziwitso chawo, anawapereka MULUNGU KU MTIMA WOKANIKA..."
Abale tandivetserani mwa uzimu pa mfundo yakuti "Anawapereka(Anthu Ochimwa) Ku Mtima Wokanika" 📖 Aroma 1:28,...✍️✍️
MULUNGU akamudzudzula muthu ochimwa maulendo ochuluka, ndipo MULUNGU akaona kuti muthu ochimwayu sakusiyabe makhalidwe onyasa