26/12/2024
yathu ya Lero.
Ife a Malawi Eyes Online, sitikudabwa ndi pang'ono pomwe ndi zomwe Anthu maka otsatira chipani cha MCP, akuchita ponyoza ndi kutukwana Bishop wamkulu wa mpingo wa akatolika, Luke Thomas Msusa, kamba kogwilitsa ntchito ufulu wake ofotokoza maganizo ake posagwilizana ndi zotsatira za kafuku fuku wa ngozi ya ndege yomwe inapha Dr Saulosi Chilima ndi Anthu ena asanu ndi atatu (8) ku chikangawa pa 10th June.
Ife a Malawi Eyes Online, tikukumbutsa mtundu mtundu wa Amalawi, kuti Anthu otsatira chipani cha MCP, anatengera khalidwe la Akulu akulu a chipanicho, omwe ankakambirana zofuna kupha ma Bishop a mpingo wa akatolika, kamba koti iwo analemba kalata yodzudzura nkhanza za chipani cha MCP, pansi pano utsogoleri wa Kamuzu Banda, mchaka cha 1992.
"Abwere kuno ma Bishop amenewa ndipo ine ndiwakodzera, anatero Mayi Hilda Manjankhosi, yemwe anali wapambando wa Amayi m'boma la Lilongwe.
"Ndipo lero lomwe lino ma Bishop amenewa afe ndithu dzuwa lisanalowe' anatero Tuzija Phiri, yemwe anali wapambando wa chipani cha MCP, m'boma la kasungu.
Koma bwanji tisaphe ma Bishop amenewa, koma tikumane nawo ndikuchita zokambirana' anatero Kapichita Musa, yemwe anali wapambando wa chipani cha MCP, m'boma la Mangochi.
Aaaaaaaa! Kodi munthu akanyoza Bambo ake umakambirana naye? anafunsa motero Wadson Deleza, yemwe anali nduna ya Boma.
Ayiiiiij timangopha basi, Akulu akulu akale nse a chipani cha MCP pa mkumanowo anayankha motero...
Lero lomwe lino dzuwa lisanalowe ma Bishop amenewa akaoname ndi Mulungu wawo, anagwilizana motero kuti ma Bishop onse aphedwe chifukwa cha kalata yodzudzura nkhanza za Boma, lomwe analemba pa 8th March mchaka cha 1992.
Ngati sitikudabwa ndi kutukwanidwa komanso kunyongedwa kwa Bishop Thomas Luke Msusa, umboni ulipo kuti chipani chawo cha MCP chomwe chinkafuna kupha ma Bishop a mpingo wa akatolika.
Kuti mutipeze mwachangu ndipo mudzimva nkhani zochitika pa Dziko lonse lapansi kuphatikizapo nkhani za nkhondo. Copied from MW eyes online