17/05/2024
Wachiwiri kwa wa pampando wa komiti wa masapota a timu ya FOMO m'chigawo chapakati, Peter Malata, ali kuchipatala komwe akulandira thandizo pomwe wavulazidwa ndi anthu ena omwe akuganiziridwa kuti ndiotsatira timu ya Creck Sporting.
Malingana ndi mlembi wa mkulu wa komiti ya masapota a FOMO kuchigawo chapakati, Felix Guga, wati anthu oganiziridwawa anafika pa bwalo la Civo kudzachita zomwe akukhulupilira kuti ndizazikhulupiliro zawo pamapeto pazokonzekera za timu ya FOMO.
Koma atakanizidwa kulowa mu bwalo la zamaseweroli, anthuwa adayamba kumenya wachitetezo wa FOMO komanso Malata ndipo mwa mwayi wachitetezoyi adathawa pomwe Malata wavulazidwa, ndipo adatengeredwa kuchipatala komwe akulandira thandizo.
Tinayesera kuti tiyankhule ndi mlembi wamkulu wa timu ya Creck Sporting, Aaron Mtaya, koma anati timuimbire pakapita ola imodzi chifukwa choti ali pansewu.
Tikhala tikukupatsirani zambiri